Hymn 156
I love the Lord, the fount of life & grace
Author unknown
Hymn 156
I love the Lord, the fount of life & grace
Author unknown
Verse 1
Ndikonda Mlungu pomva Mbuye wanga
Amva pemphero ndi kulira kwanga,
Namachereza khutu nditapfuula,
Andithandiza, nandipulumutsa.
Verse 2
Mulungu wanga ndiye wachifundo
Ndi wolungama mtima ndi wabwino;
Apulumtsa anthu akufoka,
Akathandiza nkhawa imachoka.
Verse 3
Mtimanga, bwera kuti upumule,
Wakuchitiranso zokoma Mbuye,
Wakuchotsera imfa ndi misozi,
Ndingakhumudwe asungira phazi.
Verse 4
Nditani ine kubwezera Mbuye
Zokoma zonse anandichitira?
Chipulumutso chake ndidzatama,
Ndinalumbira zija ndidzapatsa.
Verse 5
Imfa ya anthu ake imkomera,
Awalandira m’nyumba zokonzeka.
Mbuye, kapolo wanu ndipereka